1 Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,
4 Zingwe za imfa zinandizinga;
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda;
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi;
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka;
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga;
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano,
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine,
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga;
45 Iwo onse anataya mtima;
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;