1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu,
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya,
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,