1 Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,
2 Pemphero langa lifike pamaso panu;
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni
9 maso anga ada ndi chisoni.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;
16 Ukali wanu wandimiza;
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;