1 Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;
2 Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,
3 Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,
4 ‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.
5 Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,
6 Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?
7 Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;
8 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?
9 Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;
10 Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;
11 Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;
12 Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;
13 Mkono wanu ndi wamphamvu;
14 Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;
15 Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,
16 Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;
17 Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo
18 Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,
19 Kale munayankhula mʼmasomphenya,
20 Ndamupeza mtumiki wanga Davide;
21 Dzanja langa lidzamuchirikiza;
22 Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;
23 Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake
24 Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,
25 Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,
26 Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,
27 Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;
28 Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,
29 Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,
30 “Ngati ana ake adzataya lamulo langa
31 ngati adzaswa malamulo anga
32 Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,
33 Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,
34 Sindidzaswa pangano langa
35 Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga
36 kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya
37 udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,
38 “Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,
39 Mwakana pangano ndi mtumiki wanu
40 Inu mwagumula makoma ake onse
41 Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;
42 Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;
43 Mwabunthitsa lupanga lake,
44 Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake
45 Mwachepetsa masiku a unyamata wake;
46 “Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?
47 Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa
48 Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?
49 Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,
50 Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,
51 mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,
52 “Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”