1 Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,
2 Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.
3 Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,
4 Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,
5 Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,
6 Yehova imvani pemphero langa;
7 Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,
8 Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;
9 Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga
10 Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;
11 Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,
12 Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;
13 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;
14 Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;
15 Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,
16 Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;
17 Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu