1 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano,
4 ili ndi lamulo kwa Israeli,
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo;
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani,
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu;
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
11 “Koma anthu anga sanandimvere;
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
13 “Anthu anga akanangondimvera,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;