1 Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.
3 Koma olungama asangalale
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo
11 Ambuye analengeza mawu,
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro;
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto,
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko,
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero;
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri,
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka,
18 Pamene Inu munakwera mmwamba,
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani;
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu,
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu;
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo;
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu;
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera,
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu;
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu,
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango,
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto;
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu,
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika;