1 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,
17 Iwe umadana ndi malangizo anga
18 Ukaona wakuba umamutsatira,
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,