1 Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,