1 Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;