1 Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga,
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova
5 Pereka njira yako kwa Yehova;
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso;
11 Koma ofatsa adzalandira dziko
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama
13 koma Ambuye amaseka oyipa
14 Oyipa amasolola lupanga
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova,
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota;
20 Koma oyipa adzawonongeka;
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko,
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu,
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa,
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu;
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama
29 olungama adzalandira dziko
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru,
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake;
32 Oyipa amabisala kudikira olungama;
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo
34 Khulupirira Yehova,
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso;
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama;
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka;
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova;
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa;