1 Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;
2 Tengani chishango ndi lihawo;
3 Tengani mkondo ndi nthungo,
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera,
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira,
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro,
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;
19 Musalole adani anga onyenga
20 Iwowo sayankhula mwamtendere,
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu