1 Weruzeni Inu Yehova
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
7 kulengeza mofuwula za matamando anu
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta