1 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
9 Yehova ndi wabwino kwa onse;
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
16 Mumatsekula dzanja lanu
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.