1 Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga;
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,