1 Tamandani Yehova.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
6 Ndithu sadzagwedezeka;
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;