1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake;
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;
3 Munyadire dzina lake loyera;
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;
15 “Musakhudze odzozedwa anga;
16 Iye anabweretsa njala pa dziko
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula,
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto;
24 Yehova anachulukitsa anthu ake;
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake,
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina
45 kuti iwo asunge malangizo ake