1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala;
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake,
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake;
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala;
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa,
8 Inu munamiza mapiri,
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa,
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa;
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo;
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi;
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba;
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye,
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu,
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino,
17 Mbalame zimamanga zisa zawo;
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale;
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,
21 Mikango imabangula kufuna nyama,
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu
28 Mukazipatsa,
29 Mukabisa nkhope yanu,
30 Mukatumiza mzimu wanu,
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya;
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera,
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi