1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena,
3 Tsono popeza iwe mwana wanga
4 Usagone tulo,
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje,
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe;
7 Zilibe mfumu,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono
11 umphawi udzakugwira ngati mbala
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa,
13 amatsinzinira maso ake,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa;
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo,
17 maso onyada,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako;
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse,
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira;
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama,
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake,
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi
27 Kodi munthu angathe kutenga moto
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri,
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo,
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa,
35 Iye savomera dipo lililonse;