1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
21 Usayiwale malangizo angawa,
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
25 Maso ako ayangʼane patsogolo;
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;