Provérbios 4

NYA

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu;

2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.

3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;

4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,

5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;

6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.

7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.

8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;

9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;

10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,

11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.

12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;

13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.

14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa

15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;

16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;

17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi

18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha

19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;

20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;

21 Usayiwale malangizo angawa,

22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza

23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu

24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;

25 Maso ako ayangʼane patsogolo;

26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako

27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado