1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga?
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu,
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko,
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa,
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira
12 Masiku onse a moyo wake
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;
17 Iye amavala zilimbe
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,
19 Iye amadzilukira thonje
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu;
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake;
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda,
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;
26 Iye amayankhula mwanzeru,
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala;
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita