1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;
3 Sindinaphunzire nzeru,
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo,
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri
16 Manda, mkazi wosabala,
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake,
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,
22 Kapolo amene wasanduka mfumu,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu
27 dzombe lilibe mfumu,
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,