Eclesiastes 1

NYA

1 Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:

2 “Zopandapake! Zopandapake!”

3 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse

4 Mibado imabwera ndipo mibado imapita,

5 Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa

6 Mphepo imawombera cha kummwera

7 Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,

8 Zinthu zonse ndi zotopetsa,

9 Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,

10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,

11 Anthu akale sakumbukiridwa,

12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.

13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!

14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;

16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”

17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.

18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado