1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake,
7 Wolemera amalamulira wosauka,
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,
13 Munthu waulesi amati,
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu
21 malangizo okudziwitsa zolungama
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake
26 Usakhale munthu wopereka chikole
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?