1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola;
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango;
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano,
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera;
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya,
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo,
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino;
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo,
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga;
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake,
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona,
13 Usakonde tulo ungasauke;
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.”
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali,
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu,
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu;
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake,
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba,
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!”
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova;
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova,
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,”
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova;
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu;
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo,
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa,