1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,
13 amene amasiya njira zolungama
14 amene amakondwera pochita zoyipa
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,