1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa
11 Akadzati, “Tiye kuno;
12 tiwameze amoyo ngati manda,
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali
14 Bwera, chita nafe maere,
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;
20 Nzeru ikufuwula mu msewu,
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu,
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.
25 Uphungu wanga munawunyoza.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;