1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza,
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;
21 Choyipa chitsata mwini,
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,