1 Efereimu amadya mpweya;
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda;
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;
8 Efereimu amadzitama ponena kuti,
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako
10 Ndinayankhula ndi aneneri,
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa?
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.