1 Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi,
2 Ndani adzandipatsa malo
3 “Amapinda lilime lawo ngati uta.
4 “Aliyense achenjere ndi abwenzi ake;
5 Aliyense amamunamiza mʼbale wake
6 Iwe wakhalira mʼchinyengo
7 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti,
8 Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa;
9 Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi?
10 Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri
11 Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja,
12 Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
18 Anthu akuti, “Abwere mofulumira
19 Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti,
20 Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova;
21 Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu
22 Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti,
23 Yehova akuti,
24 koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi:
25 “Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”