1 Tsono Yobu anayankha kuti,
2 “Achikhala mavuto anga anayezedwa,
3 Ndithu, zikanalemera kupambana mchenga wa ku nyanja;
4 Mivi ya Wamphamvuzonse yandibaya,
5 Kodi bulu wakuthengo amalira akakhala ndi msipu,
6 Kodi chakudya chosakoma nʼkuchidya chopanda mchere,
7 Zakudya zimenezi sindifuna nʼkuzilawa komwe;
8 “Aa, ndikanalandira chimene ndikuchipempha,
9 achikhala chinamukomera Mulungu kuti anditswanye,
10 Pamenepo ine ndikanakhalabe ndi chitonthozo ichi,
11 “Kodi mphamvu zanga nʼzotani kuti ndizikhalabe ndi chiyembekezo?
12 Kodi ine ndili ndi mphamvu?
13 Kodi ndili ndi mphamvu zodzithandizira ndekha,
14 “Munthu amene ali kakasi ayenera kukhala ndi abwenzi odzipereka,
15 Koma abale anga ndi wosadalirika ngati mitsinje yowuma msanga,
16 Ali ngati mitsinje ya madzi akuda nthawi ya dzinja,
17 koma madziwo amasiya kuyenda nthawi yachilimwe,
18 Anthu oyenda pa ngamira amapatukirako kufuna madzi;
19 Anthu oyenda pa ngamira a ku Tema amafunafuna madzi,
20 Amataya mtima chifukwa ankayembekezera kupeza madzi;
21 Tsono inunso mukuonetsa kuti ndinu osathandiza,
22 Kodi ine ndinanenapo kuti, ‘Ndiperekereni kenakake,
23 ndilanditseni mʼdzanja la mdani,
24 “Phunzitseni, ndipo ine ndidzakhala chete;
25 Ndithu, mawu owona ndi opweteka!
26 Kodi inu mukufuna kundidzudzula pa zimene ndikunena,
27 Inu mungathe kuchita maere kuti mugulitse ana amasiye
28 “Koma tsopano ndichitireni chifundo pamene mukundiyangʼana.
29 Fewani mtima, musachite zosalungama;
30 Kodi pali choyipa chilichonse pa milomo yanga?