1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?
2 Mkwiyo umapha chitsiru,
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake,
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,
11 Iye amakweza anthu wamba,
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana;
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,
26 Udzafika ku manda utakalamba,
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,