1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse;
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;
30 Ana ake amayamwa magazi,