Jó 38

NYA

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:

2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga

3 Onetsa chamuna;

4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi?

5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa!

6 Kodi maziko ake anawakumba potani,

7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi

8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa,

9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake

10 pamene ndinayilembera malire ake

11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire

12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa,

13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi

14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo;

15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa,

16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja

17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa?

18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa?

19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti?

20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi?

21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale!

22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana

23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto

24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani

25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula,

26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu,

27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa

28 Kodi mvula ili ndi abambo ake?

29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani?

30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala,

31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi?

32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake

33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa?

34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo

35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime?

36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima,

37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo?

38 pamene fumbi limasanduka matope,

39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi

40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo

41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado