1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
8 Zirombo zimakabisala
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
14 “Abambo Yobu, tamvani izi;
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,