1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali;
4 Ndithudi mawu anga si abodza;
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita,
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,
12 Koma ngati samvera,
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;
14 Amafa akanali achinyamata,
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;
19 Kodi chuma chanu
20 Musalakalake kuti usiku ubwere,
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake
25 Anthu onse amaziona ntchitozo;
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe!
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo,
28 mitambo imagwetsa mvulayo
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera,
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse,
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani,
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho;