1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;
3 Pakuti khutu limayesa mawu
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,
6 Ngakhale ndine wolungama mtima,
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’
19 Iye sakondera akalonga
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,
27 Chifukwa anasiya kumutsata
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;