1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula;
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba,
5 Mundiyankhe ngati mungathe;
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi,
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva,
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa,
18 kumulanditsa munthu ku manda,
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,
21 Thupi lake limawonda
22 Munthuyo amayandikira ku manda,
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere;