Jó 32

NYA

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.

2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.

3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.

4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.

5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;

8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,

9 Si okalamba amene ali ndi nzeru,

10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;

11 Ndadikira nthawi yonseyi,

12 ineyo ndinakumvetseranidi.

13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;

14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,

15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;

16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,

17 Inenso ndiyankhulapo tsopano;

18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri,

19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,

20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;

21 Sindidzakondera munthu wina aliyense,

22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado