1 “Koma tsopano akundinyoza,
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine,
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala,
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa,
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo,
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma,
7 Ankalira ngati nyama kuthengo
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina,
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe;
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa;
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa,
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane;
13 Iwo anditsekera njira;
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka,
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu;
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo;
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa;
19 Wandiponya mʼmatope,
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha;
21 Inuyo mumandichitira zankhanza;
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo;
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa,
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima,
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera;
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka;
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa;
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe,
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka;
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro,