1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi,
3 pamene nyale yake inkandiwunikira
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri,
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane,
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka,
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda
8 anyamata amati akandiona ankapatuka
9 atsogoleri ankakhala chete
10 anthu otchuka ankangoti duu,
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga,
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo,
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa;
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa;
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya;
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi;
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga,
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi,
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine,
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi,
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso;
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira;
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu;