1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi,
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu;
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho;
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,
9 Iye amaphimba mwezi wowala,
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera,
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja;
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga,
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake;