1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;
16 Mulungu walefula mtima wanga;
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,