1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;
7 Sunawapatse madzi anthu otopa,
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;
22 Landira malangizo a pakamwa pake
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera,
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,