1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza,
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso;
10 Ana ake adzabwezera zonse
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake
13 ngakhale salola kuzilavula,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza;
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo
17 Sadzasangalala ndi timitsinje,
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha,
21 Palibe chatsala kuti iye adye;
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;
23 Akadya nʼkukhuta,
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana,
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,