1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti,
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri;
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera,
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha;
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa;
9 Iye wandilanda ulemu wanga
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu;
11 Wandikwiyira ndipo
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu,
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga;
14 Abale anga andithawa;
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo;
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha,
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga;
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza;
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane;
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha;
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni,
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo,
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo,
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka,
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji,
29 Inu muyenera kuopa lupanga;