1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima,
13 moti ukupsera mtima Mulungu
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;