1 “Munthu wobadwa mwa amayi
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu;
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo:
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake