1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi,
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa;
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse
4 Koma inu mukundipaka mabodza;
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu!
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga;
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni?
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo;
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule;
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira;
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa
17 Mvetserani mosamala mawu anga;
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga,
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane?
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi,
21 Muchotse dzanja lanu pa ine,
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha,
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati?
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo.
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa,