1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake,
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani?
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo;
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi;
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako,
17 Moyo wako udzawala kupambana usana,
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo;
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza,